Wailesi ya Nyungwe yakhazikitsa maere omwe pakutha pa tsiku anthu oposera makumi atatu azikhala akuchita mphumi yopambana ndalama yosachepera 10,000 kwacha

Maerewa akhazikitsidwa lachitatu pa 21 may 2025 pamene wailesiyi yamaliza zokambilana zake ndi kampani yochititsa maere ya Supa win

Malingana ndi yemwe akuedetsa za maelewa M’modzi mwa ogwira ntchito kuchokera pa wailesi ya Nyungwe Robert Benson Malenga wati maelewa azitchulidwa kuti Nyungwe Supa win omwe kulowa kwake ndi kuimba *4348 * 26 # pa lamya ya mmanja

Kuonjezera apo omwe akutenga mbali yochita maelewa akuenera kukhala ndi ndalama yosachepera 500 kwacha Ku mpamba kapena Airtel money yomwe iziwathandizira kugura tikiti yolowera mu maelewa ndikukhala pa ndandanda wa anthu omwe azikhala akuchita mphumi nthawi iliyonse yomwe maelewa akuchitika.

Olemba Martha Chirwa M’biza

#Liwu la M’chigwa

All reactions:

10Moses Moyala and 9 others

Related posts

Boma la Malawi kudzera ku khonsolo ya boma la Chikwawa lakweza pantchito aphunzitsi a m’sukulu za pulayimale pafupifupi 900 a m’bomali.

Bungwe la center for human rights, Education,Advice and Assistance (CHREAA) lalangiza ophinzila achitsikana kuti azinena za nkhanza zogonana zomwe amakumanazo kwa adindo.

CHIPATALA CHA MAKHUWIRA CHILI PA CHIOPSEZO CHA MADZI OSEFUKIRA