SUKULU YOMWE UTUMIKI WA TIRDEM IKUMANGA IDZATCHULIDWA DZINA LOTI GUARDIAN CHRISTIAN ACADEMY

Utumiki wa Time of Repenting and Deliverance ku Domasi ukumanga sukulu ya Sekondare m’mudzi mwa Senior Group Namira mfumu yaikulu Mulilima ku Chikwawa.

Mkulu wa TIRDEM, mtumwi Albert Mpende watiuza kuti Utumikiwu wachita izi podziwa kuti maphunziro ndi ofunikira maka pa chitukuko cha dziko la Malawi.

Iye amayankhula izi Lolemba pa 24 March 2025 pomwe Nyungwe FM imafufuza mwachidwi zomwe zimamveka zoti Utumikiwu wayamba kumanga sukulu yoyambira makalasi a Form 1 mpaka 4.

Padakali pano ntchitoyi ili mkati ndipo ikadzatha sukuluyi idzatchedwa Guardian Christian Academy.

Wolemba: Jaison Chiyembekezo

#Liwu_la_Mchigwa

Related posts

Wailesi ya Nyungwe yakhazikitsa maere omwe pakutha pa tsiku anthu oposera makumi atatu azikhala akuchita mphumi yopambana ndalama yosachepera 10,000 kwacha

Boma la Malawi kudzera ku khonsolo ya boma la Chikwawa lakweza pantchito aphunzitsi a m’sukulu za pulayimale pafupifupi 900 a m’bomali.

Bungwe la center for human rights, Education,Advice and Assistance (CHREAA) lalangiza ophinzila achitsikana kuti azinena za nkhanza zogonana zomwe amakumanazo kwa adindo.