Magulu a alimi mzimbe a Kasinthula Can Growers Association m’boma la Chikwawa, pa 10 Epulo 2025 asankha Amade Alide kukhala wapampando wa alimiwa.

Alimi a mzimbe okwana 762 ndi omwe atenga nawo mbali pa chisankhochi chomwe chinachitikira ku maofesi a zaulimi a Kasinthula pa msonkhano waukulu wa pa chaka wa alimiwa.

Wapampando wa Khonsolo ya m’bomali, a Martin Goche, womwe anali mlendo wolemekezeka alangiza adindo atsopanowa kuti aziyika zinthu poyera kuti alimi a mzimbe azipeza phindu lochuluka.

Atangosankhidwa pa udindowu, Amade Alide ati awonetsetsa kuti alimi akulandira ndalama zochuluka pa phindu lomwe amagawana kuti mabanja awo akhale otukuka.

Mlangizi wamkulu ku Unduna wa Zamalonda ndi Mafakitale, a Levi Longwe, apempha atsogoleri ongosankhidwa kuti azitsatira malamulo aboma oyendetsera magulu a zaulimi.

Pa chisankhochi, a Richard Mkomba asankhidwa kukhala wachiwiri kwa wapampando, a James Chiwambo apeza udindo wa mlembi ndipo wotsatira awo ndi a Stella Dzimwani pamene udindo wa msungichuma wapita kwa a Biyesi Chibowo.

Wolemba: Francis Mwale

Related posts

Mpingo wa Time of Repenting and Deliverance Ministries (TIRDEM),wapereka mbewu ya chimanga kwa amayi amasiye ndi okalamba

NZIKA ZACHITA ZOKAMBIRANA NDI ACHITETEZO

Kampani ya Illovo Sugar Malawi mogwirizana ndi bungwe la Catholic Relief Services (CRS) komanso boma la malawi yamanga nyumba zomwe ndizolimbana ndikusitha kwa nyengo.