Bungwe la center for human rights, Education,Advice and Assistance (CHREAA) lalangiza ophinzila achitsikana kuti azinena za nkhanza zogonana zomwe amakumanazo kwa adindo.

wanena izi ndi modzi mwa akuluakulu ku bungweli,mayi Hope Gee Williams pa mwambo olimbikitsa ufulu wa anthu,womwe unachitikila pa sukulu ya sekondale ya St Michaels boma la chikwawa.

Mayi Williams ati bungweli lachita izi pozindikila kuti atsikana ambili amabisa za nkhanza zomwe amakumana nazo tsiku ndi tsiku.ndipo mayi Williams ati nkumanowu unali wofunika kwambili kamba kuti wathandizila kuzindikilitsa atsikanawa zakuyipa kwa ma ukwati awana achichepele.

Mayi Williams alangiza ophunzilawa kuti akhazikitse ma gulu oti azithandizana komanso kulimbikitsana pa nkhani ya zamaphunzilo

wolemba:Robert Benson Malenga

Related posts

Wailesi ya Nyungwe yakhazikitsa maere omwe pakutha pa tsiku anthu oposera makumi atatu azikhala akuchita mphumi yopambana ndalama yosachepera 10,000 kwacha

Boma la Malawi kudzera ku khonsolo ya boma la Chikwawa lakweza pantchito aphunzitsi a m’sukulu za pulayimale pafupifupi 900 a m’bomali.

CHIPATALA CHA MAKHUWIRA CHILI PA CHIOPSEZO CHA MADZI OSEFUKIRA