TRACK YATSEKA MSEWU PA KAMUZU BRIDGE BOMA LA CHIKWAWA

#Nyungwe_FM_Nkhani

Galimoto yonyamula katundu ya mtundu wa track panopa, yatseka msewu pa chipata cha malo ochitira chipikiseni cha apolisi pa Kamuzu Bridge m’boma la Chikwawa.

Woyendetsa galimotoyo a Ganert Nyirenda, wauza Nyungwe FM kuti ngoziyi yachitika galimotoyi italephera kukwera mtunda kamba kusokonekera kwa magiya zomwe zinachititsa kuti ibwerere m’mbuyo.

Galimototoyi yomwe nambala yake ndi NE4410 inanyamula matumba 600 a simenti yomwe imachokera ku Blantyre ndi kukatula kwa Ngabu.

Wolemba: Francis Mwale

#Liwu_la_Mchigwa

Related posts

Wailesi ya Nyungwe yakhazikitsa maere omwe pakutha pa tsiku anthu oposera makumi atatu azikhala akuchita mphumi yopambana ndalama yosachepera 10,000 kwacha

Boma la Malawi kudzera ku khonsolo ya boma la Chikwawa lakweza pantchito aphunzitsi a m’sukulu za pulayimale pafupifupi 900 a m’bomali.

Bungwe la center for human rights, Education,Advice and Assistance (CHREAA) lalangiza ophinzila achitsikana kuti azinena za nkhanza zogonana zomwe amakumanazo kwa adindo.