Bungwe la Community Focus (COFO) Lachitatu pa 26 March 2025 lapereka zipangizo zophunzirira pa sukulu ya pulayimare ya Matchombe.

Bungwe la Community Focus (COFO) Lachitatu pa 26 March 2025 lapereka zipangizo zophunzirira pa sukulu ya pulayimare ya Matchombe m’dera la zamaphunziro la Boma m’boma la Chikwawa.

Mkulu wa bungweli, a Joshua Malunga awuza wailesi ya Nyungwe kuti apereka ma yunifolomu komanso nsapato kwa ophunzira amasiye komanso ovutikitsitsa okwana 60.

A Malunga ati aperekanso mabuku, makopo ndi zolembera ndi cholinga choti maphunziro apite patsolo m’boma la Chikwawa.

Wolemba: Chifundo Bwalamba

#Liwu_la_Mchigwa

Wojambula zithunzi: COFO

All reactions:

1414

Related posts

Wailesi ya Nyungwe yakhazikitsa maere omwe pakutha pa tsiku anthu oposera makumi atatu azikhala akuchita mphumi yopambana ndalama yosachepera 10,000 kwacha

Boma la Malawi kudzera ku khonsolo ya boma la Chikwawa lakweza pantchito aphunzitsi a m’sukulu za pulayimale pafupifupi 900 a m’bomali.

Bungwe la center for human rights, Education,Advice and Assistance (CHREAA) lalangiza ophinzila achitsikana kuti azinena za nkhanza zogonana zomwe amakumanazo kwa adindo.