AMUMANGA ATATAYIRA KHANDA M’CHIMBUDZI

#Nyungwe_FM_Nkhani

Kwa Ngabu m’boma la Chikwawa, apolisi ati amanga mayi ena a zaka 27 kamba kotayira mwana wobereka wokha m’chimbudzi chokumba kamba koti mwamuna wake adakana pathupi pa mwanayo.

Mneneri wa apolisi m’bomali, Sergeant Dickson Matemba wati maiyu adapalamula mlanduwu pa 23 March 2025 m’mudzi mwa Thobwa kwa Mfumu yaikulu Ngabu m’bomali.

Padakali pano apolisi m’bomali omwe adzudzula mchitidwewu ati atengera maiyu ku bwalo la milandu ndi kukayankha pa mlandu womwe akumuganizira kuti wapalamula.

Wolemba: Francis Mwale

#Liwu_la_Mchigwa

Related posts

Wailesi ya Nyungwe yakhazikitsa maere omwe pakutha pa tsiku anthu oposera makumi atatu azikhala akuchita mphumi yopambana ndalama yosachepera 10,000 kwacha

Boma la Malawi kudzera ku khonsolo ya boma la Chikwawa lakweza pantchito aphunzitsi a m’sukulu za pulayimale pafupifupi 900 a m’bomali.

Bungwe la center for human rights, Education,Advice and Assistance (CHREAA) lalangiza ophinzila achitsikana kuti azinena za nkhanza zogonana zomwe amakumanazo kwa adindo.