Ntchito yomanga malo osambira pa chipatala chaching’ono cha Chavala m’dera la Mfumu yaikulu Kasisi m’boma la Chikwawa yayamba Lolemba pa 17 March 2025.

#Nyungwe_FM_Nkhani

Ntchito yomanga malo osambira pa chipatala chaching’ono cha Chavala m’dera la Mfumu yaikulu Kasisi m’boma la Chikwawa yayamba Lolemba pa 17 March 2025

Malingana ndi amene wapereka thandizo la ntchitoyi, Patrick Kampira yemwenso ndi Shadow MP wa UTM Kumpoto kwa Chikwawa wati wachita izi pokhudzika ndi kuperewera kwa malo osambira pa chipatalachi.

Kampira wati ndi khumbo lake kuti akadzapambana pa chisankho cha pa 16 September 2025 kudzatukula ntchito za umoyo pa chipatalachi ndi zipatala zonse za Kumpoto kwa Chikwawa.

M’modzi mwa zzika za derali a Edwin Moda ayamikira zomwe Kampira wachita ponena kuti mavuto aukhondo pa chipatalachi tsopano achepa.

Wolemba: Jaison Chiyembekezo

#Liwu_la_Mchigwa

Related posts

Wailesi ya Nyungwe yakhazikitsa maere omwe pakutha pa tsiku anthu oposera makumi atatu azikhala akuchita mphumi yopambana ndalama yosachepera 10,000 kwacha

Boma la Malawi kudzera ku khonsolo ya boma la Chikwawa lakweza pantchito aphunzitsi a m’sukulu za pulayimale pafupifupi 900 a m’bomali.

Bungwe la center for human rights, Education,Advice and Assistance (CHREAA) lalangiza ophinzila achitsikana kuti azinena za nkhanza zogonana zomwe amakumanazo kwa adindo.